Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Anthu a ku Ntcheu ndiwothokoza – Nyakwawa Gwedeza

Nyakwawa yayikulu Gwedeza yaku Ntcheu yati anthu m’bomali ndiwokondwa ndi chitukuko chokulitsa msewu wa M1 pa Kampepuza.

A Gwedeza ati mwachitsanzo, chifukwa cha kuonongeka kwa msewu, pa msika wa Kampepuza pamachitika ngozi zomwe tsopano zikuyembekezeka kuchepa.

Pa Kampepuza ndi amodzi mwa malo odziwika bwino m’boma la Ntcheu kaamba ka msika omwe umachitika lachisanu lililonse.

Ntchito yokonzanso ndikukulitsa msewuwu inayamba mu September chaka chatha ndipo ikuyembekezeka kutha mu November chaka chino.

Related posts

Amuna ambiri kumpoto akudwala khansa ya chida cha abambo

Alinafe Mlamba

ESCOM yayamika Chakwera chifukwa cha $21 million

Romeo Umali

Kalembera wa voti ali mkati

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.