Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Technology

Mgwirizano wamphamvu pakati pa MACRA, ogwira nawo ntchito ndi ofunika — Kunkuyu

Nduna yofalitsa nkhani a Moses Kunkuyu ati pakufunika m’gwirizano wa mphamvu pakati pa bungwe la Malawi Communications Regulatory Authority (MACRA) ndi mabungwe amene amagwira nawo ntchito pofuna kuti ntchito zofalitsa uthenga zipite patsogolo.

A Kunkuyu amafotokoza izi mu mzinda wa Blantyre pamene amatsegulira msonkhano wa sabata imodzi wa bungwe la MACRA ndi ma bungwe amene amagwira nawo ntchito.

Iwo anati zikatere zipereka danga kwa ma bungwe komanso kuti amvetsetse ntchito za MACRA komanso m’mene angagwilire ntchito limodzi pofuna kukweza luso lofalitsa ma uthenga pogwiritsa ntchito zipangizo za makono.

Mkulu wa bungwe la MACRA, a Daud Suleman, anati dziko la Malawi likhazikitsa malamulo atsopano omwe azitsogolera momwe mabungwe komanso anthu azigwiritsira ntchito zipangizo maiuthenga mogwirizana ndi luso la makono.

Mwambo ngati omwewu ukhalaponso m’mizinda ya Lilongwe ndi Mzuzu.

 

Related posts

Chikwawa eye specialist wins international humanitarian award

Rabson Kondowe

Kulila kwa mafoni ochuluka kwagwiritsa mbava

Alinafe Mlamba

President Chakwera wakhazikiska Committee ya nduna kwendeska nyifwa ya Chilima

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.