Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Ophunzira ena a Form Four achedwa kulemba mayeso awo lero

Ophunzira ena amene akulemba mayeso a Form Four ku Mangochi achedwa kulemba mayeso awo mmawa walero kaamba kakuti mapepala a mayeso amene amafuna kulemba sanafike.

Malinga ndi mmodzi mwa aphunzitsi amene akuyang’anira nawo mayesowa ku Mangochi, ophunzirawa akuwasunga mzipinda zolembelamo mayeso pamene akuluakulu a ofesi ya zamaphunziro ali mkati mwa ntchito yoonetsetsa kuti mapepala a mayesowa afike.

Ena mwa malo olembetsera mayeso amene akhudzidwa ndi Mangochi Secondary komanso sukulu yasekondale yoyendera ya Mpondasi.

Mneneri wa bungwe la Maneb, Angela Kashitigu, wati mapepala olembera mayesowa anasochera potumizidwa m’boma la Chikwawa mmalo mwa Mangochi.

Pakadali pano, bungweli akuti likukonza za vutoli.

Ophunzirawa akuyembekezeka kulemba phunziro la Physics.

Wolemba: Owen Mavula

Related posts

Amabera anthu powanamiza kuti amachulukitsa ndalama

Romeo Umali

NEEF yapereka feteleza wa ngongole kwa alimi

Rabson Kondowe

Mlimi watola chikwama

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.