Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Bus ya Bullets inakalibe mmanja mwa khothi

Bus ya FCB Nyasa Big Bullets sinabwerere kuma ofesi atimuyi, dzulo italandidwa ndi ma Sherrif.

Bus-yi inalandidwa kaamba koti timuyi inali ndi ngongole ya ndalama zokwana K25 million ndi mphunzitsi wawo wakale Franco Ndawa.

Malingana ndi modzi mwa akuluakulu a Bullets, a Albert Chigoga, timuyi yalipira ndalamayi kuphatikizapo K4 million ndipo akudikira ndondomeko zokhudza malamulo kuti bus-yi ibwerere zomwe akuyendetsa ndi owayimira pamilandu.

Chigoga watsutsaso kuti timuyi ili ndi malingaliro ochotsa osewera ena pazifukwa kuti akupangila dala kuti timuyi isamachite bwino.

Lachiwiri, osewera a Bullets anakana kuchita zokonzekera za timuyi.

 

By Praise Majawa

Related posts

Education Ministry lauds World Relief for promoting technical education

Romeo Umali

Gwengwe describes SACCOs as catalyst for economic recovery

Rabson Kondowe

Agency opens window of opportunity to artists

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.