Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Zotsatira za mayeso a sitandade 8 ndi fomu 2 zatuluka

Unduna wa zamaphunziro mogwirizana ndi bungwe loona za mayeso la Malawi National Examinations Board (MANEB) ati mwa ophunzira a sitandade 8 okwana 252, 448 omwe analemba mayeso, ophunzira okwana 217,708 ndi omwe akhonza kuyimira 86.16% kusiyana ndi chiwerengero cha chakachatha cha 87.87% chomwe chinali chokwera.

Wapampando wa bungwe la MANEB a Dorothy Nampota ati ophunzira a fomu 2 okwana 163,950 omwe analembetsa, ophunzira 154,504 ndi omwe analemba mayesowa, ndipo 110,102 ndi omwe akhonza kuyimira 71.20% pomwe chaka chatha chiwerengero china 72.65%.

Nduna yazamaphunziro a Madalitso Kambauwa Wirima yayamikira bungwe la MANEB kamba kogwiritsa ntchito njira zamakono pantchito yawo yolembetsa mayeso komanso kutulutsa zotsatira za mayesowa munthawi yake.

A Kambauwa ati ophunzira omwe alemba mayeso akupulamaile a sitandade 8 ali ndikuthekera kowona ngati asankhidwa kapena ayi kudzera pa intaneti.

 

Related posts

‘Ogwira ntchito za luso lamanja chepetsani utambwali’

Rabson Kondowe

Chionetsero cha kanema chilipo mu November

Romeo Umali

Dziko la Malawi lili ndi mwai waukulu woonjezera Mphamvu zamagetsi

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.