Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Ngozi za kabaza zikuchulukirabe

Kutsatira kuchuluka kwa imfa komanso ngozi zapamsewu zodza kaamba ka kabaza, bungwe lamadotolo owona za mafupa pamodzi ndi abwenzi osiyanasiyana akupitilira kufotokozera komanso kuphunzitsa anthu m’dziko muno malamulo komanso mmene angapewere ngozizi.

Bungweli lachititsa msonkhano ku Area 25 m’boma la Lilongwe lero, pomwe pali adindo osiyanasiyana ndipo akukambirana zokhudza chitetezo chapamsewu, maka muntchito za kabaza.

Malinga ndi bungweli, anthu 48 pa 100 aliwonse m’dziko muno amakhala ndi ulumali akachita ngozi yakabaza zomwe ati ndizodandaulitsa.

Wachiwiri kwa nduna ya zaumoyo, a Halima Daud, ati vuto langozi zakabaza likuchititsa kuti zipangizo zachipatala zidzichepa poti anthu ovulala akumakhala ochuluka.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

LUANAR holds first White Coat Ceremony

Doreen Sonani

Apostle Kawinga aids hunger stricken families in CK

Jeffrey Chinawa

Katanda to launch book on mental health

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.