Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Wapha mwana wa zaka zitatu chifukwa chodutsa mmunda mwake

Apolisi ku Chiradzulu amanga John Tebulo wazaka 43 pomuganizira kuti wapha mwana wazaka zitatu kaamba kodutsa mmunda mwake.

Ofalitsankhani wapolisi ku Chiradzulu, Cosmas Kagulo, wati makolo a mwanayo analawilira kumunda kumusiya akugona kaamba koti mundawo unali pafupi.

Atadzuka, mwanayo anayamba kulondola makolo akewo ndipo anadutsira m’munda mwa Tebulo.

Izi sizinamusangalatse ndipo anatenga chikwanje ndikuyamba kukhapa mwanayo, yemwe anthu anathamangira naye kuchipatala koma mwatsoka, anali atamwalira.

Apolisi apulumutsanso woganiziridwayo kaamba koti anthu ammudzi anayamba kumumenya moti akulandira thandizo kuchipatala atavulala kwambiri.

Izi zachitika m’mudzi wa Likhomo, mfumu yaikulu Sandrack m’boma la Chiradzulu.

 

Olemba: Charles Pensulo

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

MCP gears for 2025 Elections

Mayeso Chikhadzula

MET predicts favourable rainy season

MBC Online

NBM sponsors MDF military drill

Paul Mlowoka
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.