Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Wapha mwana wa zaka zitatu chifukwa chodutsa mmunda mwake

Apolisi ku Chiradzulu amanga John Tebulo wazaka 43 pomuganizira kuti wapha mwana wazaka zitatu kaamba kodutsa mmunda mwake.

Ofalitsankhani wapolisi ku Chiradzulu, Cosmas Kagulo, wati makolo a mwanayo analawilira kumunda kumusiya akugona kaamba koti mundawo unali pafupi.

Atadzuka, mwanayo anayamba kulondola makolo akewo ndipo anadutsira m’munda mwa Tebulo.

Izi sizinamusangalatse ndipo anatenga chikwanje ndikuyamba kukhapa mwanayo, yemwe anthu anathamangira naye kuchipatala koma mwatsoka, anali atamwalira.

Apolisi apulumutsanso woganiziridwayo kaamba koti anthu ammudzi anayamba kumumenya moti akulandira thandizo kuchipatala atavulala kwambiri.

Izi zachitika m’mudzi wa Likhomo, mfumu yaikulu Sandrack m’boma la Chiradzulu.

 

Olemba: Charles Pensulo

Related posts

NGORA recommits to strengthening civil society

Romeo Umali

Dedza adds junior primary school

Romeo Umali

Msonkhano waukulu tichita mu September — JB

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.