Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani Politics

Msonkhano waukulu tichita mu September — JB

Prezidenti wa chipani Cha PP, Dr Joyce Banda walengeza kuti chipanichi chidzakhala ndi msonkhano wake waukulu pa 7 September chaka chino mumzinda wa Lilongwe.

Iwo alengeza izi ku Nancholi komwe anachititsa msonkhano wandale.

Iwo ati ndi okondwa kuti chipani cha PP ndi champhamvu ku Blantyre ndipo apempha owatsatira kuti apitirize kusunga bata.

Khwimbi la anthu linasonkhana kumsonkhanowu pabwalo la Nancholi ndipo nawo aGeorge Nnesa, mtsogoleri wa chipani Cha Mafunde, analinso nawo pa msonkhanowu.

Olemba: Blessings Cheleuka
#MBCDigital
#Manthu

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Agro-dealers urged not to sell counterfeit seeds

MBC Online

First Lady distributes relief items in Nkhotakota

Beatrice Mwape

MALAWI TO RAISE K15 BN FROM CEMENT

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.