Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

UTM yapempha mgwirizano pa nthawi ya maliro

Chipani cha UTM chati ndipofunika kuti pakhale umodzi pakati pa anthu onse m’dziko muno pofuna kuti mwambo wokhuza wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino malemu Dr Saulos Chilima ndi anthu ena omwe anali nawo mu ndege yomwe inagwa lolemba mu nkhalango ya Chikangawa, uyende bwino.

Ofalitsankhani za chipanichi, A Felix Njawala anena izi pa msonkhano wa atolankhani omwe akuluakulu a chipanichi anachititsa ku Iikulu la chipanichi ku Area 10 mu mzinda wa Lilongwe.

Iwo apemphanso a Malawi kuti apewe mchitidwe wotumizirana zithunzi za ngoziyi kudzera mmasamba a mchezo.

Pa msonkhanowu panalinso mlembi wamkulu wa chipanichi, a Patricia Kaliati.

Thupi la malemu a Chilima likuyembekezeka kudzayikidwa m’manda Lolemba ku Nsipe m’boma la Ntcheu.

Related posts

District councils urged to enforce spatial plans for development

Romeo Umali

Malawi secures K140 billion to foster development

Rabson Kondowe

MRA PLEDGES CONTINUOUS INNOVATION

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.