Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

A Chilima adatukula kampani yathu ya Airtel — Kamoto

Mkulu wa kampani ya Airtel Malawi, Charles Kamoto, wati malemu Dr Saulos Chilima anali munthu wodzipereka ndi wokonda ntchito.

Poyankhula ndi MBC, a Kamoto ati kampani ya Airtel Malawi sidzaiwala zazikulu zomwe adachita posintha kagwilidwe ka ntchito kumpaniyi.

“Ma tower ambiri omwe mukuwaona m’dziko muno a Airtel, malemu a Chilima ndi omwe adathandizira kuti ayike malo osiyanasiyana,” anatero a  Kamoto.

Iwo anati adaphunzira zinthu zambiri kuchokera kwa malemu Dr Chilima.

Malemu Dr Chilima adagwilako ntchito ku kampani zosiyanasiyana m’dziko muno, kuphatizapo Airtel Malawi, asadayambe kuchita za ndale.

 

Print Friendly, PDF & Email

Author

  • Mayeso Chikhadzula joined MBC in 2006, he's an Investigative Journalist and Principal Reporter. He's also a News Anchor, Presenter, and producer.

Related posts

Tisewera kuti tibwezeretse ulemu wathu – Mabedi

Paul Mlowoka

CHAKWERA MALAWI BOUND

Blessings Kanache

LOCAL FIRMS READY TO PARTNER WITH GOSHEN CITY

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.