Anthu oposa 146,000 a m’maboma a Ntcheu ndi Balaka akuyembekezeka kukhala ndi madzi abwino komanso aukhondo kudzera ku ntchito yopopa madzi mu nthaka pogwiritsa ntchito mphamvu ya dzuwa, pansi pa ndondomeko ya Mpira-Balaka Water Supply System.
Izi zadziwika pamene wachiwiri kwa nduna yoona za madzi, a Liana Kakhobwe Chapota, anayendera malo opopa madziwa a Njereza komanso Bawi m’bomali.
Malinga ndi undunawu, pakadalipano boma layika mipopi yoposa 1600 m’boma la Ntcheu ndipo mwa mipopiyi, 1214 yayamba kale kugwira ntchito.
A Chapota ati boma likufunitsitsa kuti pofika 2030, aMalawi ochuluka athe kupeza madzi abwino komanso aukhondo mosavuta.
Pakadalipano, mkulu wa za madzi ku Ntcheu, a Onanses Nyirenda, ati apeza ndalama zoti zithandizire kugula ma paipi oonjezera kuti athe kupereka madzi abwino wa kwa anthu ochuluka m’bomali.
Bungwe la World Bank, mogwirizana ndi boma, linaika ndalama zoposa K140 billion kuti zithandizire anthu ku ngozi zogwa mwa dzidzidzi ndipo mwa ndalamazi, K1.4 billion anaipatula kuti amangire Mpira – Balaka water supply system.