Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Ulendo wotsiriza wa Dr Chilima wayambika kupita ku Nsipe

Galimoto yomwe yanyamula malemu Dr Saulos Chilima kubwalo lazamasewero la Bingu National lanyamuka pa mdipiti kupita kumudzi kwawo kwa Mbirimtengerenji mdera la mfumu yaikulu Champiti ku Nsipe m’boma la Ntcheu.

Prezidenti wa dziko lino, Dr Lazarus Chakwera komanso mayi wa dziko lino Madam Monica Chakwera ndiwo anatsogolera mtundu wa a Malawi popereka ulemu wotsiriza kwa malemu Dr Chilima.

Thupi la Malemu Dr Chilima akaliyika m’manda mawa Lolemba, lomwe a Prezidenti a dziko lino akhazikitsa kuti likhale tsiku la tchuthi.

Related posts

WAIPHULA!

Blessings Kanache

Oyendetsa galimoto wadzipereka atapha anyamata atatu

Romeo Umali

Save The Children yapereka mbaula zamakono ku Lilongwe

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.