Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Politics

Tiyeni tipitirize kumvera mtsogoleri komanso kukonda chipani chathu — Msukwa

Wapampando wa komiti yomwe yakonza msonkhano waukulu wa chipani cha Malawi Congress a Kezzie Msukwa walangiza mamembala a chipanichi kuti apitirize kukhala pambuyo pa Prezidenti Dr Lazarus Chakwera, yemwenso ndi mtsogoleri wa chipanichi.

A Msukwa alangizanso mamembala a chipanichi kuti apitirize kusunga mwambo mchipani komanso kumvera mtsogoleri wa chipanichi.

Iwo ati ali ndi chikhulupiliro kuti chipani cha MCP chidzapambana pa chisankho cha chaka chamawa.

Olemba: Isaac Jali ndi Olive Phiri

Related posts

TIGWIRANE MANJA NDI BOMA PA CHITUKUKO -MATOLA

MBC Online

‘Tikufufuza’

Romeo Umali

Deposit Insurance Corporation ayikhazikitsa sabata lamawa

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.