Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

‘Titsitsa mitengo ya ufa wopangira bread’

Mmodzi wa akuluakulu a kampani zopanga bread za Nyanja Bakery, Olympic Bakery komanso BreadTalk, Saizi Bakali wati ndiokonzeka kutsitsa mtengo wa bread mokomera a Malawi ngati kampani zopanga ufa wa tiligu zingatsitse mtengo ogulira ufawu.

Bakali wanena izi pamene akulukulu akampani zosiyanasiyana akukumana ndi nduna yaza malonda ndi mafakitale, a Sosten Gwengwe komanso mkulu wa banki yayikulu m’dziko, a MacDonald Mafuta Mwale komwe akukambirana zotsitsa mitengo ya katundu osiyanasiyana.

Mkulu wa kampani yopanga ufa ya Bakhresa, a Rao Pattipati Bakhresa wati ndiwokhutira ndi zokambirana zomwe zachitika lachitatu ndi a Gwengwe ndi a Mwale.

A  Bakhresa ati a Malawi ayembekezere kuti pofika sabata ya mawa anthu awona kusintha kwakukulu pa msika.

Iwo ati malinga ndi zomwe a Reserve Bank awatsimikizira, zinthu ziyenda bwino posachedwapa.

Ena mwa omwe akukumana nawo nkuphatikizapo opanga bread ndi ufa wa bread, kampani zogulitsa nkhuku ndi zakudya za nkhuku, kampani yopanga mafuta wophikira komanso kamapani zopanga sopo.

Print Friendly, PDF & Email

Author

  • Mayeso Chikhadzula joined MBC in 2006, he's an Investigative Journalist and Principal Reporter. He's also a News Anchor, Presenter, and producer.

Related posts

TNM donates to Children’s Cancer Ward at Queen Elizabeth Central Hospital

MBC Online

MDF graduates officers in health services

MBC Online

Amai atatu ali mchitokosi pamulandu wakuba ku Mangochi

Davie Umar
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.