Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Chepetsani chinyengo poweruza milandu — Mzikamanda

Mkulu wa mabwalo a milandu m’dziko muno, Justice Rizine Mzikamanda, walangiza oweruza milandu mumabwalo osiyanasiyana kuti adzilemekeza malumbiro awo pogwira ntchito yawo mwachilungamo.

A Mzikamanda anena izi pomwe amalumbilitsa oweruza milandu atsopano asanu ndi anayi omwe amaliza maphunziro awo apadera a miyezi 6 atagwira ntchito yoimira anthu pamilandu kumabungwe osiyanasiyana.

A Mzikamanda ati mdziko muno anthu ambiri akusakasaka chilungamo chomwe nthawi zambiri chimabwera mochedwa kapenanso kukhotetsedwa kumene kamba kakuchepa kwa oweruza pena kusakhulupirika pantchito kwa oweruza milandu omwe alipo kale.

M’mawu ake, m’modzi wa oweruza milandu omwe angolumbiritsidwa kumenewa, a Ramai Muhamad, anati ayesetsa kugwira ntchito mokhulupirika potsatira malamulo.

Oweluza milandu atsopanowa awatumiza m’maboma osiyanasiyana kuti athandizire pa lingaliro lofuna kukhala ndi ma Senior Resident Magistrate m’boma lilolonse m’dziko muno.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Zokonzekera za mwambo wa mapemphero okumbukira ufulu wa dziko lino zili mchimake

Beatrice Mwape

Kuchedwa kobwezeretsa ndalama zosochera kutha posachedwa

Arthur Chokhotho

MANEPO idzudzula mchitidwe wa nkhanza kwa achikulire

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.