Malawi Broadcasting Corporation
Agriculture Development Local News Nkhani

TAMA Farmers Trust yayamikira boma pa mitengo yabwino ya fodya

Bungwe la alimi a fodya la TAMA Farmers Trust layamikira mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera poonetsetsa kuti alimi a fodya akugulidwa fodya pa mitengo ya bwino chaka chino.

Mtsogoleri wa bungweli, a Kalima Banda, ayankhula izi ku nyumba ya chifumu mu mzinda wa Lilongwe pamene alimi a fodya a m’bungweli anakumana ndi Dr Chakwera.

A Banda anapempha kuti boma liwathandize pokwanilitsa chiwerengero cha makilogaramu a fodya yemwe ogula akumufuna. Iwo anati ndi zosangalatsa kuona kuti alimi akukondwa ku msikawu kaamba ka mitengo yabwinoyi.

Mwazina, iwo anati anakakonda kuti mtsogoleri wa dziko linoyu apitilize kuthandiza poonetsetsa kuti alimiwa adzilandira ndalama zafodya yemwe agulitsa mmisika ya fodya pakangotha masiku awiri okha.

Print Friendly, PDF & Email

Author

  • Mayeso Chikhadzula joined MBC in 2006, he's an Investigative Journalist and Principal Reporter. He's also a News Anchor, Presenter, and producer.

Related posts

Level 1 Hockey Coaching Course commences in Blantyre

MBC Online

Dedza approves K45.3 billion 2025/26 budget

Sothini Ndazi

Malawi, Tanzania akondwelera Kiswahili

Emmanuel Chikonso
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.