Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Sports Sports

Sitilora kuti atichitse manyazi pakhomo — Mpinganjira

A Bob Mpinganjira, amene ndi mphunzitsi wa timu yampira wa miyendo yadziko lino koma ya achisodzera, wati iwo salola kuti timuyi ichititse anthu manyazi pamene ikhale ikuchita nawo mpikisano wa mayiko anayi omwe ukhale ukuchitika kuyambira lero masana pa bwalo lamasewero la Bingu mumzinda wa Lilongwe.

Lero ndi tsiku lotsegulira masewero kwa achisodzera ndipo ntchito iyamba pamene timu ya Malawi ithambitsane ndi timu ya Zimbabwe.

A Mpinganjira ati awuza anyamata awo kuti asakhale ndi phuma ngati akufuna kuti apambane.

Lachisanu, timu ya Kenya idzasewera ndi Zimbabwe ndipo lamulungu, Malawi idzakumana ndi Kenya amene adzakhale masewero otsiriza.

Malinga ndi malamulo a mpikisanowu, yemwe adzapeze mapointi ochuluka ndi amene adzapambane.

Poyambilira, mu gawo la achisodzera, kumayenereka kukhala mpikisano wa kaphelachoka koma udasintha kaamba kakuti timu ya Zambia ya achisodzera inanena kuti siyichita nawo mpikisanowu pazifukwa zina.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Let the police do their job — Umodzi Party

MBC Online

NCIC halts construction by Chinese company over non-compliance

Mayeso Chikhadzula

Chakwera calls for joint efforts in digital transformation

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.