Malawi Broadcasting Corporation
Development Local News Nkhani

Sitigawana katundu yemwe talanda kwa anthu ogulitsa malonda — Khonsolo ya Lilongwe

Khonsolo ya mnzinda wa Lilongwe yati sizoona kuti ogwira ntchito ku khonsoloyi amagawana katundu yemwe alanda kwa anthu ogulitsa malonda m’malo osayenera.

Mfumu yamnzinda wa Lilongwe, a Richard Banda, alankhula izi pomwe bungwe la Citizen Alliance linachita msonkhano ndi khonsoloyi okambirana zomwe khonsoloyi ikuchita pamavuto ena amunzindawu, omwe bungweli linanena kuti achitepo kanthu.

Malinga ndi a Banda, katundu yemwe amalanda kwa anthu ogulitsa malonda mmalo osayenera amamusunga ndipo amadzamugulitsa pa okushoni.

Pakadali pano, mtsogoleri wa Citizen Alliance, a Baxton Nkhoma, wati ndiokhutira kuti khonsoloyi ikuyesetsa kuthana ndi ena mwa mavuto omwe anawauza kuti achitepo kanthu.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Govt praises activist late Chiwaula

MBC Online

NYCOM hailed for youth agricultural empowerment

MBC Online

Eye expert tells parents to limit children’s screen exposure

Chimwemwe Milulu
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.