Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Sports Sports

Ellen Simwaka akufuna lamba wa WBC

Katakwe otchaya nkhonya, Ellen Simwaka, wati wayika chidwi chofuna kutenga lamba wa World Boxing Council (WBC) akapatsidwa mpata okumana ndi amene akufunanso lambayu.

Simwaka wayankhula izi pamene wabweleranso mu ring ndi chipambano atagonjetsa Jesca Mfinanga, wa m’dziko la Tanzania, kudzera pa ma points mu nkhonya imene inalipo usiku wapitawu ku Tanzania.

Osewerayu, amene amakhala m’dziko la South Africa, anati akumasowa masewero chifukwa osewera ena akumamuopa ndi kumukana kuti asewere naye.

“Yemwe ankasunga lambayu, Kudakwache Chiwandire, wa ku Zimbabwe adakana kusewera nane nkhonya yokonzakonza patangotsala masiku ochepa,” anadandaula Simwaka.

Padakalipano, katakwe pa zigogodoyu akusungira malamba akuluakulu awiri a WBF komanso International Boxing Federation komanso iye ali pa nambala yoyamba mu Africa mu gulu la Bantam Weight.

 

Related posts

Roads Authority impressed with M1 rehabilitation progress

Mayeso Chikhadzula

Real Estate described as game changer

Romeo Umali

Mchinji embraces e-payment for social cash transfer

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.