Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Namondwe Chido watuluka

Nthambi yoona za nyengo yati namondwe Chido tsopano wabwelera m’dziko la Mozambique atachepa mphamvu.

Mkulu oona za nyengo ku nthambiyi, a Lucy Mtilatila, ati namondweyu watuluka asanaononge kwambiri monga momwe amaonekera.

Iwo ayamikira anthu m’dziko muno chifukwa chosatira mwachidwi mauthenga ochenjeza omwe nthambiyi komanso nthambi zina zimapereka othandiza kuteteza miyoyo komanso katundu.

A Mtilatila ayamikiranso nthambi yoona za ngozi zogwa mwadzidzidzi ya DoDMA yomwe imathandizira kupereka mauthenga ochenjeza kudzera pa lamya za mmanja.

Pamenepa, a Mtilatila ati a Malawi akhale omasuka kaamba koti palibenso chiopsezo chilichonse cha namondweyu.

 

Olemba: Charles Pensulo

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Chipatala cha Namatumi ku Thyolo achimaliza kumanga

Blessings Kanache

Chakwera, Nyusi to open agriculture fair

Secret Segula

PAC against politicking tragic events

Timothy Kateta
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.