Malawi Broadcasting Corporation
Entertainment Local Nkhani

Oyimba zauzimu tisaike chidwi pa ndalama koma Mulungu – Kamwendo

M’modzi mwa oyimba nyimbo zauzimu m’dziko muno, Ethel Kamwendo, walangiza oyimba nyimbo zauzimu kuti asakomedwe ndi ndalama koma agwiritse maitanidwe awo pomaimba nyimbo zolimbikitsa miyoyo ya anthu omwe akusautsika ndi mikwingwilima yodza kaamba ka uchimo.

Kamwendo wati chaka cha 2024 anakhuzidwa kwambiri ati poti panali kusakanikilana kwambiri pakati pa oyimba zauzimu ndi oyimba zachikunja zomwe wati zikuika pachiopyezo kuti zitha kusungunula cholinga chenicheni cha maitanidwe.

“Sizoona kuti oyimba nyimbo zauzimu tidzingoti uku talowera uku talowera. Tidziwe kuti tili ndi maitanidwe omwe titha kuphonya pa cholinga cha Mulungu ngati sitisamala,” anatero Kamwendo.

Kamwendo watinso chaka cha 2025 iye akhala akupitiriza kuimba nyimbo zobukitsa dzina la Yesu. Iye walangizanso achinyamata kuti adzizisamala popewa mchitidwe wachisawawa monga uhule, mowa komanso kusuta kuti miyoyo yawo ikhale yaitali.

Related posts

Mayi amangidwa atamenya mwana wake mwankhanza ndikumutsira chitedze

Alinafe Mlamba

2024 Mzuzu City Executive Summit gets K5 million boost

Rabson Kondowe

Ndondomeko ya mphamvu ku anthu yachiwiri akuikhazikitsa ku Lilongwe

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.