Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Mayi amangidwa atamenya mwana wake mwankhanza ndikumutsira chitedze

Apolisi m’boma la Balaka amanga a Lilian Matako, ochokera mmudzi mwa Kanyumbaka, mfumu yayikulu Sawali m’boma lomwelo powaganizira kuti adamenya mwankhanza mwana wawo wachichepere.

Ofalitsankhani za polisi ya Balaka, a Gladson M’bumpha, wati mayiwa akuganiziridwa kuti adamenya molapitsa mwana wawo Mercy Magombo wa zaka 9, yemwe amaphunzira mu Standade 3 pa sukulu ya Ngwangwa Primary.

Mtsikanayo akuti pa 28 June chaka chino,malinga ndi mayi wakeyo, anaba ndalama yokwana K2000 imene Matako adasiya kunyumba panthawi imene amapita ku geni ndipo atafunsidwa ndikuvomera,mayiyo mothandizidwa ndi anyamata ena anamanga Mercy miyendo ndi manja ndikumumangilira ku mtengo ndipo pamapeto pake adamumenya ndikumuthira madzi osakaniza ndi chitedze.

Malume amwanayo ndiwo adakatsina khutu apolisi lero pa 6 July ndipo mayiyo akuyembekezeka kukaonekera kubwalo lamilandu posachedwapa.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Ntchito yodinda ma pasipoti yayambiranso ku Mzuzu

Emmanuel Chikonso

Promise Kamwendo wapepesa!

Romeo Umali

Apolisi agwira anthu awiri omwe akuwaganizira kuti amaba ku Area 25

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.