Malawi Broadcasting Corporation
Entertainment Nkhani

OYIMBA OMWE ANALI PANSI PA NDE’FEYO AIMBA LERO KU BLANTYRE

Zokonzekera zonse za phwando la mayimbidwe limene likutchedwa kuti Nde’feyo legacy, lomwe lichitikire ku 24/7 ku Blantyre lero, zili mchimake.

Mwambowu ubweretsa pamodzi oyimba asanu amene anasayinidwa ndi kampani ya Nde’feyo pomwe ankayamba kuyimba monga Maskal, Piksy, Onesimus, Trumel ndi Bucci.

Poyankhula ndi MBC, mmodzi wa oyimba-wa, Maskal, yemwe wabwera m’dziko muno kuchokera ku America komwe amakhala, wati anthu akonzekere mayimbidwe apamwamba.

Wolemba: Simeon Boyce

Related posts

Madotolo okonza nkhope za anthu afika

Alinafe Mlamba

A Chakwera ali mu mzinda wa Mzuzu

Alinafe Mlamba

Mwana wa Standard 5 wadzipha atamuletsa kuchita zibwenzi

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.