Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Madotolo okonza nkhope za anthu afika

Madotolo okwana khumi (10) ochokera m’dziko la America, omwe ndi akatswiri azachipatala pokonza nkhope za anthu, afika m’dziko muno kudzagwira ntchitoyi.

Malinga ndi yemwe watsogolera gulu lama dotololi, Dr Tania Nkungula, ntchitoyi, yomwe ikhale yamasabata awiri, ayigwira pachipatala cha Queen Elizabeth Central Hospital mu mzinda wa Blantyre.

” Ambiri mwa anthu [odwala] amakhala kuti mwazina ali ndi zotupa mkamwa komanso ovulala nkhope pa ngozi zosiyanasiyana,” atero Dr Nkungula.

Poyankhula atalandira alendowa pa bwalo la ndege la Chileka ku Blantyre, kazambe wadziko lino ku America, a Esme Chombo, ati madotolo wa athandiza anthu pafupifupi 40 omwe ali ndi mavuto otere.

Dziko lino lili ndi dotolo m’modzi yekha odziwa za ukadaulo otere.

Related posts

A Chakwera acheza ndi ochita malonda kunyumba ya boma

Rabson Kondowe

Makolo asiya mwana pa golosale

Blessings Kanache

Chimbale chatsopano ndichothokoza Mulungu — Thuya

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.