Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Sports Sports

Osewera wakale wa Silver Strikers wamwalira

Osewera wakale watimu ya Silver Strikers Mike Robert, wamwalira kamba kavuto la impso kuchipatala cha Kamuzu Central munzinda wa Lilongwe.

Mng’ono wake wa Mike, Jacob,yemwe amasewera mutimu ya Blue Eagles, wati mkulu wakeyu wakhala akuvutika ndi nthenda ya impso kwa nthawi yayitali.

Jacob wati Mike pakatipa anadwalanso malungo aakulu amene anathamangira ku ubongo ndipo lero chamma 4 koloko kumadzuloku ndi pamene wamwalira.

Jacob watiuza kuti padakali pano dongosolo la mwambo wa maliro silinadziwike.

Mike anakhalako mtsogoleri wa osewera atimu ya Silver ndipo amachokera m’boma la Dowa.

 

Olemba : Praise Majawa

Related posts

Amangidwa kaamba koganiziridwa kuti adagwilirira mwana

Romeo Umali

Apolisi agwira anthu awiri omwe akuwaganizira kuti amaba ku Area 25

Romeo Umali

MBC’s Top of the Class gets K10M boost from MBS

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.