Apolisi ku Lilongwe agwira anthu awiri omwe akuwaganizira kuti akukhudzidwa ndi kubedwa kwa katundu wambiri mu mzindawu komanso kuchita ziwembu.
M’neneri wa Polisi ya Kanengo, a Gresham Ngwira, ati awiriwa, a Shukulani Mussa a zaka 20 ndi ndi a Tonny Junior Juma azaka 22 akuwaganizira kuti akhala akuchita m’chitidwewu ku Area 25 B ndi madera ena ozungulira.
A Ngwira ati anthu ena akufuna kwabwino anawatsina khutu za anthuwa popeza akhala akugwiritsa ntchito ndalama mwachisawawa ndipo atafufuza anawapeza ndi katundu wambiri kuphatikizapo makanema a mtundu wa Plasma.
Awiriwa akuyembekezeka kukawonekera ku bwalo la milandu posachedwapa apolisi akamaliza kuchita kafukufuku wawo.
A Mussa amachokera m’mudzi wa Kumwembe, m’dera la mfumu yayikulu Tambala m’boma la Dedza, pomwe a Juma amachokera m’mudzi wa Mzondo m’dera la mfumu yayikulu Chitukula ku Lilongwe.
Olemba: Yamikani Makanga


