Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Ophunzira pa UNIMA akhazikitsa kampani ya luso lamakono

Ophunzira pa sukulu yaukachenjede ya University of Malawi(Unima) ku Zomba akhazikitsa chipangizo chothandiza anthu omwe ali ndi ulumali wosaona.

Mmodzi mwa ophunzirawo, Hudson Mwangalika, wati mwa zina, chipangizocho, chomwe amavala ku maso ngati magalasi, chimatulutsa phokoso yemwe wachivalayo akayandikira chinthu kutsogolo kwake. Izi zimathandiza kuti munthuyo asaombane ndi chinthucho.

Izi zadziwika pomwe ophunzirawo amakhazikitsa kampani yawo ya luso lamakono yotchedwa HB Space TL.

Pamwambowo, ophunzirawo anawonetsanso chipangizo chotayiramo zinyalala chotchedwa smart bin chomwe chimatseguka chokha mkati mwake munthu akachiyandikira komanso kuchibaibitsa. Ophunzirawo anawonetsanso zipangizo zina za luso lamakono.

Ndipo m’mau ake, mkulu oona za luso la makono mu unduna wa za maphunziro, Chomora Mikeka, wati zomwe achinyamatawa akonza, zingathandize kuchepetsa ndalama zomwe dziko lino limaononga pogula zipangizo ngati zomwezi kuchokera ku maiko akunja.

Related posts

Maranatha Academy offers K10m reward for six-point MSCE results

McDonald Chiwayula

DPP LACKS INTRAPARTY DEMOCRACY – CHAMBO

MBC Online

Malawi to receive Cholera RDT Kits — WHO

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.