Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Ndondomeko ya zachuma ikupereka chiyembekezo – World Bank

Banki yayikulu padziko lonse ya World Bank yati ndondomeko yazachuma ya dziko la Malawi yachaka cha 2024/2025 yomwe yaperekedwa sabata yatha, ikupereka chiyembekezo kuti chuma chadziko lino chibwelera m’chimake posachedwapa.

Mkulu wa bankiyi ku Malawi, a Hugh Riddel, anena izi mu mzinda wa Blantyre potsegulira mwambo opereka kafukufuku wa m’mene chuma chikuyendera mdziko muno, Malawi Economic Monitor (MEM).

A Riddel ati pali zinthu zambiri monga kuteteza chuma, kuunikanso ndondomeko yazipangizo za ulimi zotsika mtengo komanso kubwezeretsa chuma m’chimake, zimene zikuonetsa kuti zinthu zinthu zikhala bwino.

Koma iwo apemphanso boma kuti liwonetsetse kuti ngongole zomwe dziko lino lilinazo zikutsika komanso kusiyana kwa ndalama zomwe dziko lino limagwiritsa ntchito pogula katundu kunja komanso zomwe limapeza likagulitsa katundu (trade balance) kudzichepa.

Pa mwambowu palinso nduna yowona za madzi ndi ukhondo, mayi Abida Mia.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Mipingo ithokoza okumba manda ku Area 18

MBC Online

Lembetsani m’kaundula wachisankho — Mafumu

Arthur Chokhotho

MCP yadzipereka kukweza chigwa cha Shire

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.