Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Ndilimbikitsa ntchito zachitukuko — Mwase

Khansala wapampando watsopano m’dera la Mwasa ku Mangochi, a Stewart Mwase, alonjeza kuti alimbikitsa ntchito zachitukuko zomwe anaziyamba kale pa nthawi yomwe asanasankhidwe pa udindowu.

A Mwase amalankhula izi pamwambo owalumbilitsa omwe umachitika m’boma la Mangochi m’mawawu.

Iwo anapambana pa chisankho chapadera pa 23 July chaka chino ndipo anayimira chipani cha Malawi Congress (MCP).

“Ndathandizapo ntchito yomanga mijigo, mizikiti, ndi zina zambiri, ndipo pakadali pano chidwi changa chili pomanga chipatala chaching’ono chomwe chidzithandiza anthu amdera langa,” iwo anatero.

Pachisankho chapadera chosankha khansala wadera la Mwasa m’boma la Mangochi, a Stewart Mwase, anapambana atapeza mavote 1073.

 

Olemba Owen Mavula

Related posts

MoH declares end to cholera outbreak

Romeo Umali

Tobacco sales at K677 billion

Romeo Umali

Women with Special Needs Calls for Inclusiveness

Alick Sambo
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.