Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Mudzi wa aChewa autsekulira ku Lilongwe

AChewa pansi pa bungwe lawo la Chewa Heritage Foundation (CHEFO) atsekulira mudzi wa aChewa, m’mudzi wa Msampha, mfumu yaikulu Chadza m’boma la Lilongwe.

Mudzi wa aChewa ndi malo omwe aChewa, pansi pa bungwe lawo, anagula kuti adzichitirapo zochitika zosiyanasiyana kuphatikiza mwambo wokondwelera chikhalidwe chawo.

Pamwambowu pafika mafumu, anthu ochokera mmadera osiyanasiyana komanso Gule wa mkulu ochokera m’maboma omwe kumapezeka aChewa.

Mlendo olemekezeka pamwambowu ndi a Napoleon Dzombe, mmodzi wa akuluakulu odziwika bwino pa ntchito za malonda mdziko muno.

Wa pampando wa CHEFO, a Stanley Chakhumbira Khaila ati pamalowa adzakhazikitsapo, malo okopa alendo, Tourism Cultural Centre, yomwe idzakhale ndi Nyumba yosungirako mabukhu (Library), Museum komanso malo odyera, mwa zina.

Mwambowu ukuchitika pa nthawi yomwe aChewa akukonzekera mwambo wa Kulamba omwe uchitike ku Nkaika, mdziko la Zambia, komwe amapereka ulemu kwa Kalonga Gawa Undi, mfumu yaikulu ya aChewa mmaiko a Malawi, Zambia komanso Mozambique.

Olemba Yamikani Simutowe

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Dr Chilima afika m’dziko la Korea

Timothy Kateta

Madam Chakwera afika ku mwambo okumbukira tsiku la anthu achialubino

Eunice Ndhlovu

MRCS yagawa K180 million m’boma la Karonga

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.