Malawi Broadcasting Corporation
Culture Local News Nkhani Politics

Inkosi M’mbelwa yadzudzula ndale zonyozana

Inkosi ya Makhosi M’mbelwa V yati aMalawi akuyenera kupewa m’chitidwe wa ziwawa chifukwa dziko lino limakonda mtendere.

Inkosiyi imayankhula izi pa mwambo wa Umthetho ku Hora m’boma la Mzimba.

Mfumuyi inalangizanso zipani zonse za ndale ndi owatsatira, pamene masiku azisankho aluyandikira, kuti apewe ndale zonyozana chifukwa sizingamange dziko lino.

Mfumuyi inatinso iyi ndi nthawi yomwe aMalawi akuyenera kugwirana manja poonetsetsa kuti m’fundo zomwe boma linalonjeza zikukwaniritsidwa.

Olemba: Jackson Sichali

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

MALAWI BROADCASTING CORPORATION EXECUTIVE MANAGEMENT PLACEMENT: DIRECTOR OF NEWS AND CURRENT AFFAIRS

McDonald Chiwayula

PLANE CRASHES NEAR KIA

MBC Online

FAM FINES MAFCO, BANS KAFUNDA

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.