Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Dr Chakwera ayamikira anthu ku Nsanje posamukira kumtunda

Prezidenti Dr Lazarus Chakwera wayamikira anthu aku Makhanga m’boma la Nsanje kaamba kosamukira kumtunda pothawa madzi omwe akhala akuwasautsa chaka chilichonse.

Mtsogoleriyu wayamikiranso aphunzitsi polimbikira ntchito ndikumakhonzetsa ana kupita ku university, ngakhale anali atathawa msukulu zawo chifukwa cha namondwe.

Dr Chakwera amayankhula ku Makhanga komwe ayendera ntchito yomanga sukulu zatsopano.

Prezidenti Chakwera wati akumananso ndi bungwe la Give Direct, lomwe lathandiza midzi ina ku Makhanga kumanga nyumba anthu atathawa kunyumba zawo kaamba kamadzi.

Dr Chakwera wati akumananso ndi akuluakulu a bungweli kuti atsirize midzi itatu komanso kumanga sukulu yomwe inatsala.

Chaka chatha, Dr Chakwera anakumana ndi mkulu wa bungweli pomwe anapita ku America, zomwe zinathandiza kuti abwere kudzamanga nyumbazi.

Dr Chakwera ayenderanso chipatala cha Osiyana m’boma lomweli la Nsanje.

 

Olemba: Mercy Zamawa

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Malemu Shanil Dzimbiri akawayika m’manda ku Balaka

Mayeso Chikhadzula

FDH hikes Mayors’ Trophy sponsorship to K100 million

Beatrice Mwape

Increased digital banking uptake key to paperless transactions

Justin Mkweu
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.