Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Mfumu yaikulu Mkukula yayamika boma kaamba ka chitukuko cha madzi ammipopi

Mfumu yaikulu Mkukula ya m’boma la Dowa yayamika boma chifukwa chowapatsa anthu akwa Mkukula chitukuko cha madzi a m’mipopi.

Mfumuyi yati m’mbuyomu anthu mderali amavutikira madzi koma panopa zinthu zili bwino ndiponso matenda achepa m’derali.

Mfumu Mkukula yatinso ngongole zomwe boma likupereka kudzera ku bungwe la NEEF zikuthandiza anthu ambiri maka amayi ndi achinyamata kuyambitsa bizinesi ndikukhala odzidalira pachuma.

Naye phungu wadera la kummwera chakumvuma m’boma la Dowa, Halima Daudi, wayamika boma chifukwa cha ntchito zachitukuko zosiyanasiyana ndipo apempha kuti lionjezere chiwerengero cha anthu olandira thandizo la chimanga.

Iwo atinso anthu ayambapo kugula feteleza otsika mtengo.

Related posts

Chiradzulu moves to address ARV default rate

Rabson Kondowe

Old Mutual partners Sanwecka to empower youths

Romeo Umali

Sheriffs seize Bullets’ bus over K25 million debt

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.