Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

MBTS yati sikutolera magazi okwanira

Bungwe la Malawi Blood Transfusion (MBTS) lati silikutolela magazi okwanira, ofalitsa nkhani ku bungweli m’chigawo cha pakati, a Upile Kaimvi, atero.

Iwo amayankhula izi munzinda wa Lilongwe pamene mpingo wa Lilongwe CCAP Livingstonia Synod unasonkhanitsa achinyamata kuti apereke magazi ku bungweli.

“Ndipofunika kuti aliyense atengepo gawo popereka magazi. Tiyamike zomwe wapanga mpingowu, moyo wina wake upulumuka ndithu,” a Kaimvi anatero.

M’mawu ake, m’busa wa mpingo wa Lilongwe CCAP, a Nase Chunga, anati ndi udindo wa anthu opemphera kupereka magazi chifukwa kusowa kwa magazi muzipatala ndi vuto lalikulu limene boma palokha silingakwanitse kuthana nalo koma aliyense atengepo gawo.

M’modzi wa achinyamata amene anapereka nawo magazi, Cynthia Chipenda, anatsutsa zakuti munthu akapereka magazi amadwala

Iye anati aka kanali kachitatu iye kupereka magazi koma sanadwale.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Komiti yakunyumba yamalamulo yakhutira ndikuthetsedwa kwa mlandu wa a Chilima

Olive Phiri

Malemu Lapukeni awayika lero

MBC Online

Dr Chakwera adzudzula anthu opondereza pa ntchito ya mtukula pakhomo

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.