Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

MBS yatsegulanso sitolo ya Ekhaya

Bungwe la Malawi Bureau of Standards (MBS) latsegulanso sitolo ya Ekhaya ya ku Kanengo mu mzinda wa Lilongwe.

Lolemba, bungweli linatseka sitoloyi ndi zina zinayi kaamba kosatsatira ndondomeko za ukhondo zimene bungweli linakhazikitsa.

Kutsatira izi, ofalitsa nkhani ku MBS, a Wazamazama Katatu, anapempha eni sitolo m’dziko muno kuti malo awo adzikhala aukhondo.

A Katatu ati tsopano eni sitolo zimene anazitseka ayamba kukonza sitolo zawo malinga ndi m’ndandanda wa mavuto awo ndipo akufikira bungweli kuti liwayendere kuwaunika ngati akwaniritsa ndondomekozi ndi kuwatsegulira.

Iwo anati eni sitolozi akupereka chindapusa ngati chenjezo komanso phunziro kuti asadzachitenso izi.

Pakadalipano, m’modzi mwa akuluakulu a sitolo za Ekhaya, a Fanwell Khuluza, ati izi zawaphunzitsa ndipo aonetsetsa kuti sitolo za Ekhaya zikutsata ndondomeko zonse za MBS.

Related posts

GOVERNMENT ACTS FAST TO ADDRESS HUNGER -CRISIS IN MANGOCHI; AS DoDMA SAVES THE DAY

Romeo Umali

Tabitha wins Golden Boot

Romeo Umali

Vivo splashes prizes on customers

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.