Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local News Nkhani

Mayi amangidwa poganiziridwa kuti wapha mwamuna wake

Apolisi ku Lilongwe amanga a Ruth Nkhoma powaganizira kuti anapha amuna awo a Misheck Bayison powakoka ndi kupotokola ziwalo zobisika kaamba kakusamvana pa ndalama yokwana K40,000 imene bambowa adamwera mowa.

Malinga ndi ofalitsankhani wa Polisiyi, a Hastings Chigalu, mayiyu ataona kuti mwamuna wake wafa, anakonza ngati kuti adadzipha yekha podzimangilira koma madotolo atapima thupi la malemuwa anatsutsa izi.

A Bayison anali a m’mudzi wa Nyenyezi kwa mfumu yayikulu Malemia m’boma la Nsanje pomwe a Nkhoma amachokera m’mudzi wa Thonyiwa kwa mfumu yayikulu Nsabwe m’boma la Thyolo.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

‘Siyani kufalitsa nkhani zabodza pa imfa ya Dr Chilima’

Timothy Kateta

BT residents urged to safeguard water project infrastructure

MBC Online

Farmers urged to adopt local climate-resilient seeds

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.