Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Chikho cha Mayor’s chafika kumapeto ku Mzuzu

Bwalo lazamasewero la Katoto lero latangwanika chifukwa kukuchitika ndime yotsiriza ya chikho cha Mayor’s cha masewero a Mpira wamiyendo komanso wamanja.

Mwambowo wayamba ndi ulendo wa ndawala kuchoka kuma office a Mzuzu City Council kuyenda mu Highway kukafika pabwalo lazamasewero la Katoto.

Ena mwa amene anali nawo pa ulendowu ndi Mayor wa Mzinda wa Mzuzu a Kondwani Nyasulu, mkulu oyendetsa ntchito za mu mzindawo a Gomezgani Nyasulu, ma Khansala, ndi adindo ena osiyanasiyana kuphatikizapo akukuakulu a bank ya FDH amene akuthandiza chikhochi ndi ndalama zokwana K17 million.

Matimu a primary school a Zolozolo akumana ndi Chibavi mu masewero a mpira wa manja, pamene matimu a Mzuzu CCAP akumana ndi Katoto Primary School mu ndime yotsiliza ya Mpira wamiyendo wa anyamata.

 

Olemba: Hassan Phiri

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

NBM sees K72 billion profit

MBC Online

Statutory corporations urged to maximise profits

Davie Umar

COSAFA organisers ponder on tournament dates

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.