Bungwe la Admarc tsopano lidzigula chimanga pa mtengo wa K700 pa kilogramme (K35,000 pa thumba la 50 kilogrammes), malinga ndi mkulu wa bungweli, a Daniel Makata.
Mtengowu wakwera kuchoka pa K650 pa kilogramme (K32,500 pa thumba lolemera 50 kilogrammes) umene boma linakhazikitsa ngati poyambira.
A Makata ati Admarc yachita izi pofuna kuwonetsetsa kuti alimi akupindula ndi ulimi monga boma likufunira.