Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Mavuto ndiwo akulimbikitsa mchitidwe odzipha- Chiluzi

Mkulu woona za zamaphunziro a zachuma ku Old Mutual a Bernard Chiluzi ati anthu ambiri amene akukhuzidwa ndi mchitidwe odzipha m’dziko muno akuchita izi kaamba ka mavuto a zachuma.

A Chiluzi anena izi ku Lilongwe pa mwambo okhazikitsa bungwe la Rhema Manifest lomwe ati lidziika pamodzi achinyamata a mipingo yosiyanasiyana ndikuwaphunzitsa zokhudza moyo kuphatikizapo zachuma.

Mneneri Patson Gondwe yemwe wayambitsa guluri wati ndizomvetsa chisoni kuti achinyamata mumipingo saphunzitsidwa mbali zonse za moyo, zomwe zikuchitsa kuti anthu adziyang’anira pansi mipingo poganiza kuti anthu opemphera amayenera kukhala osauka.

“Sizoona kuti anthu akaona munthu opemphera ali ochita bwino adziganiza kuti ndi opembedza satana. Tikufuna achinyamata akhale odzidalira paokha powaphunzitsa mbali zonse za moyo,” anatero a Gondwe.

Pamwambowu panali akuluakulu a mabungwe, a zamalamulo, a katswiri oyimba nyimbo zauzimu komanso akuluakulu a mipingo yosiyanasiyana.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Tambala Super Cup launch set

MBC Online

Bungwe la MEC lalowa mu mgwirizano obwerekana katundu ndi bungwe la ECZ

MBC Online

Mlingo wa kukwera mtengo kwa zinthu (inflation) watsika mu February

Justin Mkweu
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.