Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Kukhala madyelero pomwe asilamu akukondwelera Eid

Pamene asilamu padziko lonse mawa pa 10 April 2024 akhale akuyembekezera kukondwelera Eid-Al-fitr, kusonyeza kumaliza kwa nyengo yakusala kudya ya Ramadan, gulu la achinyamata achisilamu la Y San Inspirations, motsogozedwa ndi Tariq Khamisa, lakonza zochitika monga zoyimbayimba zamasewero ndi madyelero ngati mbali imodzi yachikondwelerochi.

Polankhula ndi MBC, Khamisa wati akuyitana anthu osiyanasiyana osati asilamu okha ku zochitikachitikazi mumzinda wa Blantyre.

“Anthu omwe adzabwere ku mwambowu adzapindulanso pophunzitsidwa zomwe angachite pa nthawi yomwe akukumana ndi mavuto komanso momwe angagwilitsire ntchito luso lomwe ali nalo kupeza ndalama,” Watero Khamisa.

Gululi linajambula kale nyimbo ziwiri zotchedwa Moyowu ndi Shukura, zomwe cholinga chake ndikupereka chilimbikitso kwa anthu omwe akukumana ndi mavuto osiyanasiyana, kuphatikizapo omwe ali ndi malingaliro ofuna kuzipha.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

JUDGES TO RETIRE AT 70

McDonald Chiwayula

Police Officers drilled on new Land Laws, LIMS

MBC Online

ESCOM drills boreholes in Neno and Mwanza under MOMA Project

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.