Malawi Broadcasting Corporation
Development Health Local News Nkhani

Achinyamata awapempha kuti athandize boma pa chitukuko

Bungwe la Chiwalo Youth Network lalangiza achinyamata a m’boma la Phalombe kuti athandize kulimbikitsa ukhondo m’makomo mwawo komanso m’malo a boma monga ku Polisi ndi ku chipatala.

Wapampando wa bungweli, a Patrick Makwale, ndi amene ananena izi pamene achinyamata ena amagwira ntchito yosesa pa chipatala cha boma cha Nambazo komanso Polisi ya Nambazo m’bomalo.

A Makwale anati ndi okondwa poona kuti achinyamata ambiri ku Phalombe akuonetsa chidwi pa ntchiito za chitukuko, potukula miyoyo yawo komanso ntchito za boma.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

MWASADZU IRRIGATION SCHEME TO REDUCE HOUSEHOLD CHALLENGES IN DEDZA

MBC Online

JUDGES TO RETIRE AT 70

MBC Online

WFP ROLLS OUT LEAN SEASON CASH, FOOD DISTRIBUTION  TO CYCLONE FREDDY SURVIVORS

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.