Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News

Immigration iyamba kusindikiza ma Passport mawa

Ntchito yosindikiza ma Passport tsopano iyambanso mawa lachitatu ku Blantyre, Nthambi yoona zolowa ndikutuluka m’dziko muno, ya Immigration, yatsimikiza zimenezi.

Mneneri wa nthambiyi, a Wellington Chiponde, ati anthu onse ofuna ziphaso zoyendera, tsopano atha kuyamba kupita ku likulu la nthambiyi ku Blantyre kukapeza ziphasozi kuyambira tsikuli.

A Chiponde athokoza anthu m’dziko muno kamba kopilira pa nthawi imene nthambiyi imakonza zinthu kuti ziyambenso kuyenda bwino.

Anthu ofuna ziphaso akhala akumakatenga ziphasozi ku Lilongwe a Immigration atasiya kusindikiza ku Blantyre atathetsa mgwirizano ndi kampani yomwe inkapanga ziphasozi mmbuyomu.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

CS-EPWP hailed for improving livelihoods in Likoma

MBC Online

Malawi mourns with Namibia — President Chakwera

MBC Online

Miyoyo ya anthu ikusintha- Kawinga

Paul Mlowoka
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.