Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Ifenso tikuthandiza pa ntchito zokopa alendo —Daza

Mmodzi wa anthu  ochita malonda ogulitsa zakudya zophika zachi Malawi a Aubrey Daza, amene ndi mwini wa malo odyera a Chanza Take Away m’boma la Ntcheu, wati nawo amalonda ang’ono ang’ono mgawo  lawoli akuthandiza pantchito  zokopa  alendo.

Iwo anena izi pomwe mwezi uno, dziko lino likukumbukira ntchito zokopa alendo.

A Daza ati pakadali  pano, a Malawi ambiri anamvetsesa ubwino wa kudya  zakudya zachikhalidwe, zimenenso zikuchititsa kuti ntchito zawo ngati amalonda zidziyenda bwino.

Mmodzi mwa anthu amene tinakumana nawo pa malowa, a Julius Phiri, amene anali pa ulendo ochokera mu mzinda wa Mzuzu, anati ndiokhutira ndi momwe malo ang’ono ang’ono ngati otere akulimbikitsira ntchito zokopa alendo pogulitsa zakudya zachiMalawi.

 

Wolemba: Geoffrey Chinawa ndi Chisomo Break

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Man arrested for attempted murder of own children amid divorce

Romeo Umali

Nyasulu ndi mfumu yatsopano ya mnzinda wa Mzuzu

Rudovicko Nyirenda

Jiya wayamikira chitukuko, wadzudzula mchitidwe oononga

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.