Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

FDH Bank yathandiza NFRA ndi chimanga

FDH Bank yapeleka chimanga chokwana matani 100 ku bungwe la National Food Reserve Agency (NFRA).

Mkulu wa zamalonda ku Banki ya FDH, a Levie Nkunika, wati achita izi potsatira pempho la mtsogoleri wa dziko lino loti dziko lino lili pa ngozi yanjala.

M’mawu ake, mkulu wa bungwe la NFRA, a George Macheka, wati ndikofunika kugwiranamanja pa ntchito yothandiza mabanja amene akhudzidwa ndi njala m’dziko muno.

Malinga ndi NFRA, dziko lino likufunika pafupifupi ma tani 200,000 kuti lithane ndi vuto lanjara.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Bwalo la Magistrate lidakamvabe mboni pa m’landu wa a Chisale 

Madalitso Mhango

‘Anthu achikulire akhale ndi mwayi ovota’

MBC Online

Zokonzekera gawo lachiwiri lokonza sikimu ya Mlambe zili mchimake

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.