Malawi Broadcasting Corporation
Culture Local Local News Nkhani

Achewa athira nsembe

Anthu a chikhalidwe cha a Chewa athira nsembe ku Nsinja m’boma la Lilongwe ndipo apempha mphambe kuti akwaniritse zosowa zawo.

Kumwambowu, umene unalipo Loweruka, kunali anthu ochuluka amitundu yosiyanasiyana ya m’dziko muno komanso akuluakulu ochokera ku unduna wa zokopa alendo, unduna waza chikhalidwe ndi amene amayendetsa bungwe la Chewa Heritage Foundation, amene amatsogolera mwambowu.

Mwambowu ndi umodzi mwa miyambo ya a Chewa umene umachitika chaka ndi chaka ndipo umathandiza kubweretsa umodzi ndi mtendere pakati pa anthu amitundu yosiyana amene amakumana pa mwambowu.

Olemba: Ida Chiwaya

Related posts

‘Align budgets to Malawi2063 aspirations’

Romeo Umali

AFRICAN STUDENTS FOR MORE DIGITAL INCLUSION

Mayeso Chikhadzula

Red Cross sets aside K240 million for food insecure households in Mzimba

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.