Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Dziko la Malawi tsopano liri ndi mtsogoleri wa masomphenya – Mkaka

Mlembi wa mkulu wa chipani cha MCP a Eisenhower Mkaka wati dziko la Malawi ladala chifukwa liri ndi mtsogoleri wa masomphenya.

A Mkaka anena izi ku mwambo okondwelera kuti bungwe la NEEF lakwanitsa kubwereketsa ngongole zokwana K100 billion.

Mlembiyu wati Dr Chakwera wayambitsanso sitima yofika ku Lilongwe patatha zaka 21 sitima-yi itasiya, ndipo kubweranso kwa mayendedwe apa njanji kuthandiza kuti ngongole za NEEF zipindulire anthu m’dziko muno.

Iwo ati n’chifukwa chake anthu a kwa M’baluku ku Mangochi kwa nthawi yoyamba asankha khansala wa chipani cha MCP.

Olemba: Blessings Cheleuka

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Aliyense atenge gawo posamala misika — Khonsolo ya Lilongwe

Foster Maulidi

Mamembala a COMSIP alimbikitsa ukhondo m’misika

Doreen Sonani

Perekani mauthenga achisankho mosakondera – MEC

Simeon Boyce
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.