Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Dziko la Malawi tsopano liri ndi mtsogoleri wa masomphenya – Mkaka

Mlembi wa mkulu wa chipani cha MCP a Eisenhower Mkaka wati dziko la Malawi ladala chifukwa liri ndi mtsogoleri wa masomphenya.

A Mkaka anena izi ku mwambo okondwelera kuti bungwe la NEEF lakwanitsa kubwereketsa ngongole zokwana K100 billion.

Mlembiyu wati Dr Chakwera wayambitsanso sitima yofika ku Lilongwe patatha zaka 21 sitima-yi itasiya, ndipo kubweranso kwa mayendedwe apa njanji kuthandiza kuti ngongole za NEEF zipindulire anthu m’dziko muno.

Iwo ati n’chifukwa chake anthu a kwa M’baluku ku Mangochi kwa nthawi yoyamba asankha khansala wa chipani cha MCP.

Olemba: Blessings Cheleuka

Related posts

Sparc Systems ithandiza msonkhano wokambirana zomanga mizinda yamakono

Romeo Umali

‘Mgwirizano ndi ofunika pa ntchito yobwezeretsa chilengedwe’

Rabson Kondowe

‘Ofesi ya khonsolo ya Mangochi yatsopano idzathandiza koposa’

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.