Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Ayamba kumanga anthu ogulitsa “ambuye tengeni”

Apolisi mchigawo chakummwera ati tsopano ayamba kumanga anthu onse omwe akugulitsa mowa owopsa wa ‘ambuye tengeni’ omwe waphetsa anthu asanu kwa Manase ku Blantyre.

Anthu ena atatu ali m’chipatala.

Mneneri wa a polisi mchigawochi, a Joseph Sauka, ati apolisi ali kale mmadera osiyanasiyana komwenso akulanda mowawu, omwe ati ndi owopsa kwambiri.

“Cholinga chathu ndikuteteza anthu ku imfa zodza kamba kakumwa mowa osavomerezeka, omwenso ndi owopsa,” atero a Sauka.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

New chairperson for Salima vows to boost collaboration, prioritise development projects

MBC Online

MHRC calls for coordination in promoting refugee rights

MBC Online

Let’s recognise Chilembwe’s followers – Historian

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.