Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Ayamba kumanga anthu ogulitsa “ambuye tengeni”

Apolisi mchigawo chakummwera ati tsopano ayamba kumanga anthu onse omwe akugulitsa mowa owopsa wa ‘ambuye tengeni’ omwe waphetsa anthu asanu kwa Manase ku Blantyre.

Anthu ena atatu ali m’chipatala.

Mneneri wa a polisi mchigawochi, a Joseph Sauka, ati apolisi ali kale mmadera osiyanasiyana komwenso akulanda mowawu, omwe ati ndi owopsa kwambiri.

“Cholinga chathu ndikuteteza anthu ku imfa zodza kamba kakumwa mowa osavomerezeka, omwenso ndi owopsa,” atero a Sauka.

Related posts

Man jailed for stealing cancer centre equipment

Romeo Umali

UK grants Malawi about K7BN to help those affected by El Nino

Rabson Kondowe

Trade Secretary calls for media support in showcasing COMESA success

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.