Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Dr Usi ati alimbikitsa umodzi

Dr Micheal Usi, amene ndi wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino, ati achita zotheka polimbikitsa chipani cha UTM, monga mtsogoleri wachipanichi, kuti chikhale champhamvu.

Iwo ati cholinga chawo ndikukwaniritsa masomphenya a yemwe anali wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino, malemu Dr Saulos Chilima.

Dr Usi anena izi pamene amacheza ndi anthu a kumudzi kwawo kwa Golden kwa mfumu yaikulu Chikumbu m’boma la Mulanje.

Iwo atsimikiziranso anthu a m’boma la Mulanje kuti boma ladzipereka potukula miyoyo yawo, kuphatikizapo kupereka ngongole kwa ochita bizinezi.

 

Related posts

President Mutharika hails Red Cross role in disaster response

Doreen Sonani

Man jailed 10 years for endangering road users

Romeo Umali

Maliro a malemu Everess Kayanula anyamula mawa

Blessings Kanache
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.