Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Tiyeni titukule dziko – Dr Usi

Wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino Dr Michael Usi atsimikizira anthu aku Mulanje kuti alandira ngongole zoti achitire bizinesi ndicholinga chotukula miyoyo yawo.

Wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko linoyu wapemphanso anthu kuti alimbikitse umodzi pa chitukuko.

Iwo ati adindo akuyenera alembe anthu ochita bizinesi zing’onozing’ono mosayang’ana chipani kuti aliyense apindule.

Pa nkhani ya chakudya, Dr Usi ati iwo ali okonzeka kuthandiza anthu achikulire mdera lakwa Golden ndi chakudya pomwenso bungwe la DODMA likhale likuthandiza anthu ndi chakudya, maka omwe alibiletu.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

NYCOM splashes K100 million grants for youth

Davie Umar

Apolisi agwira mayi atamenya ogwira ntchito mu ndege

Mayeso Chikhadzula

Cultural festivals are crucial for tourism — Mzuzu City Council

Rudovicko Nyirenda
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.