Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Boma la Balaka aliyamikira polimbikitsa ntchito za umoyo

Akuluakulu a ofesi ya zaumoyo ku khonsolo ya boma la Balaka awayamikira polimbikitsa ntchito yoonetsetsa kuti anthu akulandila thandizo la zachipatala mosavuta.

Nduna ya za umoyo a Khumbize Chiponda amalankhula izi m’bomali, pomwe amatsegulira zipinda zatsopano zosamalira odwala zomwe khonsoloyi yamanga pachipatala chachikulu chaboma.

Ntchitoyi aigwira pogwilitsa ntchito zina mwa ndalama zochokera kuthumba lapadera lomwe makhonsolo akulandila kuchokera ku boma kuti zithandizile kukonza komanso kumanga malo othandizila ntchito za umoyo.

Mwa zina, khonsoloyi ikumanganso chipatala chochilira amai oyembekezela kwa chiyenda usiku, pofuna kuchepetsa ulendo omwe amaiwa amayenda kuti akapeze thandizo ku chipatala chachikulu.

Wolemba: Owen Mavula

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Favoured Martha wathandiza ana asukulu ovutika 23

MBC Online

Dr Chakwera apereka K5 million zothandizira pamaliro a Kasambara

Chisomo Manda

Dr Chakwera adzudzula mchitidwe wa chidodo pa ntchito

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.